Masalimo 82

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

2“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?

3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0