Masalimo 114

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,

2Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.

3Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;

4mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.

5Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?

6inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?

7Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,

8amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0