Masalimo 126

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0