Masalimo 70

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.

2Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.

3Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.

4Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”

5Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0