Masalimo 128

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0