Masalimo 6

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.

2Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.

3Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

4Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda?

6Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.

7Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

8Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.

9Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.

10Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0