Masalimo 113

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.

2Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.

4Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.

5Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?

6amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?

7Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;

8amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.

9Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0