Masalimo 124

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Biblica)

1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,

2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,

3iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;

4chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,

5madzi a mkokomo akanatikokolola.

6Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.

7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.

8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

Masalimo

Open the interactive reader to switch translations, adjust type, and mark verses — or browse verses by topic.

© 2002, 2016 Biblica, Inc. · CC BY-SA 4.0